Wamangawa
(Aroma 1:11-15)
Chikhulupiliro cha a kristu ndi chikhulupiliro choti upereke – chikhulupiliro chomwe chimapereka zonse – monga umo mzimayi aperekera kwa mwana wake, uwu ndio mtima omwe mtumwi Paulo anali nao kwa oyera mtima ku Mpingo wa ku Roma.
1. Chifukwa chodziperekera mwaiwe wekha
Paulo anafunitsitsa kuona mpingo wa ku Roma ndi cholinga chakuti okhulupilira akabale zipatso, Zipatso izi zikuthanthauza kubvumbulutsidwa kwa zipatso za Mzimu Woyera, kutembenuka ku tchimo ndi kukhaka ndi moyo wachiyero, ndi kupulumutsa komanso kukulitsa miyoyo yambiri. Ena amadziona ngati kukula kumachitika chifukwa cha kuthekera kwao ndi maimidwe ao kuchokera ku ntchito za manja ao, koma akristu oona amabala chipatso mwa Ambuye ndi kubala zipatso chifukwa chogwiritsidwa ntchito ndi Ambuye. Sayembekedzera mphotho kuchokera ku ntchito zomwe akwanilitsa, koma mu kukula ku moyo wauzimu ndi zipatso za miyoyo yomwe akuitumikira.
2. Chifukwa chotiletsa kubwerera mbuyo
Inde, utumiki paokha umabweretsa chikondwerero. Komabe, pamene zinthu zikuyenda mosiyana ndi zoyembekedzera zathu, apa pamabwera nyengo za nkhawa, chifooko komanso kukhumudwa. Ngakhale zili chomwechi koma izi sitingazisithe. Pakuti tili amangawa ache kwa Mulungu. Chifukwa cha ngongole iyi, tapangidwa kukhala antchito a Kristu. Wantchito sachita umo afunira monga zomusangalasa iye yekha ndi kumutenga mbuye wake ngati mlendo.
3. Chifukwa chomwe palibe kusiya
Mtumwi Paulo ankadziwa kuti iye ali wamangawa kwa Mulungu. Wopatulidwa kukhala mtumwi kwa amitundu, anakwanilitsa udindowu mokhulupirika. Ankadziwa kuti alinso wamangawa ku miyoyo yomwe iye anaitanidwa kukaitumikira. Mosafuna kukhumudwitsa Ambuye amene anakhetsa mwazi chifukwa cha iwo, anayenda mu utumiki wake mopanda kumvesera zowawa zomwe amakumana nazo ndi masautso onse. Ifenso – Chimodzimodzi , tinali anthu omwe timabweretsa zokhumudwitsa kwa Ambuye. Koma lero, tili amangawa ku ntchito iliyonse imene Ambuye akutigwiritsa mu ufumu Wake. Kufikira tsiku lomwe tidzachoka ku dziko lino, tidakali ndi ntchito yoti tigwire, osaiwala ngongole yomwe tili nayo.
Okutobala 26, 2025 Utumiki wa Tsiku la Ambuye
golowa ndi kuwala
Aroma 1:11-15
Abusa Sung-Hyun Kim


