Chikhulupiliro Molumikizana ndi Moyo
(Aefeso 6:5-9)
Akristu ambiri amakhala mu moyo wonga ngati – moyo womwe amakhala ali mu Nyumba ya Mulungu ndi moyo omwe amakhala kunja kwa Nyumba ya Mulungu ndi osiyana. Pa Tsiku La Ambuye amaonetsa onga ngati ali mu cha umulungu pamene ali mu Nyumba ya Mulungu, koma mkati mwa masiku a sabata, amakhala ochitachita ntchito za kudziko, otchera makutu ku nkhani za dziko, ndipo amatenga machitidwe athupi ngati nzeru zopambana. Koma Mulungu safuna kuti ife tidzikhala mu moyo osiyana motero.
1. Pamene tikhala opanda Chikhulupiliro
Kunena koti, ‘ntchito za nthupi zili kunja kwa chikhulupiliro,” zitha kukhala zomvesetseka – koma mu choonadi, maka zitero pofuna kuvomereza moyo odetsedwa ndi tchimo. Mulungu sakhala nafe pokhapokha pamene tili mu Nyumba yake mokha ayi, amakhala akutiona pamene tili ku malo athu onse omwe timagwira ntchito zathu, ku nyumba zathu, komanso malo onse timapezekako. Kumbali iliyonse ya moyo wathu amafunitsitsa kuti chilungamo chikaoneseredwe. Zomwe timavomereza pamene tikupembedza Mulungu sizonse timakhalamo. Moyo omwe timakhala tikutuluka pa khomo la Chalichi – umaonesera zoona za chikhulupiliro chathu.
2. Kumezedwa ndi ntchito za dziko lapansi
Anthu omwe akula akuyenda mu ntchito za ku dziko ali kunja kwa Nyumba ya Mulungu mwachizolowezi amabweretsa m’chitidwe uwu mu Nyumba ya Mulungu. M’malo mwake, kudziyenereza, kudzikonda okha, komanso nsanje zimakhazikika – osati pamene ali kunja kokha komatu ngakhale mu Chalichi. Awa amagwilitsa ntchito Mpingo kupezera zokhumba za miyoyo yao. Anthu omanena kuti amamukonda Ambuye, chonsecho amamumvetsa kuwawa mu thupi lake, omwe uli Mpingo. Mumachitidwe awo amakana chisomo cha chipulumutso, ndipo amakana ulemerero omwe timapeza mu uthenga wabwino.
3. Kusintha kuchokera mkati
Anthu pamene amva mkati mwao kuti moyo otero ndiovuta kapena owawa – amakhala akulodza wina kapena kuwada anthu ena kuleka machitidwe a iwo eni. Koma Mulungu amatiuza kuti, Zenizeni sizili mu dongosolo la dziko lapansi, koma mkati mwa mtima wa munthu – Chifukwa chimene anaperekera uthenga wabwino kwa ife sikuti zikasithe machitidwe a zinthu za dziko, koma kuti akadzutse ife ku tchimo ndipo kutitengera ku kulapa. koposa zonse – Mulungu safuna kuti tikopeke kapena kuti tikhadzikike ku ntchito zathupi koma kukhala moyo omvera ku chilungamo chake.
Abusa Sung-Hyun Kim
18 Mayi, 2025 Utumiki wa Tsiku la Ambuye
Wokhulupirika wa Chikhristu ndi Chikhalidwe cha M’dziko
Aefeso 6:5-9
Abusa Sung-Hyun Kim