Mau a Mdalitso
(Aefeso 6:23-24)
“Mau a mdalitso? Sizachidzolowedzi? Zenizeni zake ndi chiphunzitso. Ndiyenera kutuluka isanakwane nthawi ya mau a mdalitso kuti nthawi indichitire ubwino.” Kodi muli ndi maganizo otere?
1. Pangano la mphumphu
Mau a mdalitso sizitanthauza kuchita dongosolo la mapemphero mwa chidzolowedzi. Nthawi ya mau a mdalitso ndi nyengo yomwe mdalitso umakhadzikitsidwa ndi Mulungu monga analonjedza. Yemwe amapereka mau a mdalitso ndi munthu, koma ndi Mulungu yemwe anamuitana iye ndi kumupatsa ulamuliro. Ngakhale kuti mau a mdalitso amatsogoleredwa ndi munthu m’modzi, amanyamula ndi kumangilira pangano la mphumphu pakati pa Mulungu ndi anthu ake. Ngakhale kuti Mulungu amafunitsitsa kupereka mdalitso, koma ngati anthu salandira ichi, pangano ili silingathe kukwanilitsidwa. Kotero, kuti tidalitsidwe, tiyenera kuchilandira ndi chikhulupiliro ndi kumvera.
2. Kukudza mdalitso
Tikawerenga Buku la Aefeso kuchokera pomwe layambira, kumvetsera bwino zimamveka ngati mapemphero olambira, ndi pomalidzira penipeni kuthera ndi mau a mdalitso. Mau a mdalitso awa, Paulo ndi mtima wachikondi ndi mwa chiyembekedzo kwa okhulupilira ndi choti akhadzikike. Kukhumba kwake sikunali koti madalitso a Mulungu akhale pa Mpingo wa ku Aefeso okha ayi, komanso kuti kwa Mipingo yonse ya ku Asia, komanso kwa nthawi zonse. Kwa iwo omwe amakonda Yesu Kristu. Chokhumba cha Paulo chonga ichi chinakwanilitsidwe, ndiye mdalitso.
3. Mdalitso wosaonongeka
Paulo analamulira mtendere pa abale, komanso chikondi mwa chikhulupiliro, kuchokera kwa Atate, ndi kwa Ambuye Yesu Kristu. Anakhumbitsitsa kuti onse omwe ayanjanitsidwe ndi Mulungu, kuti akhale ndi moyo mwa chikhulupiliro mwa Kristu, ndiponso monga umo analandira chikondi chachikulu kuchokera kwa Mulungu, aonetsa chikondi kwa oyera mtima onse. Anakhumbitsitsa kuti kukondera kwa Ambuye kukhale kwa otero. Tiyeni timukonde Kristu ndi mitima yathu yonse. Tiyeni tilandire mdalitso osawonongeka – omwe machenjerero a ndani sangathe kuononga.
Abusa Sung-Hyun Kim
24 Ogasiti, 2025 Utumiki wa Tsiku la Ambuye
Dalitso Losatha
Aefeso 6:23-24
Abusa Sung-Hyun Kim


