Umboni wa Zinthu Zonse
(Aroma 1:20)
Kupedzeka kwa zinthu zonse kumaonetsera kuti kuli Kadaulo wina opanga zinthu mu mphamvu yosaneneka. Koma chonsecho anthu amalephera kukhulupilira mwa Iye – osati chifukwa umboni wasowa – koma mwadala amasankha kusakhulupilira.
1. Mphamvu Yamuyaya.
Mphamvu ya Mulungu – Yemwe muzonse analenga zinthu zonse ndi kudzigwirizitsa izo, ndi wamkulu kwambiri koma ovuta kumumvetsetsa. Talingalirani chinsinsi chakuya cha mbeu imakhala yaing’ono kwambiri koma ikaphuka imakula kukhala mtengo waukulu kwambiri, Komanso umo m’mene nyenyezi ziimira mu njira yake osasokera konse, Dzuwa nalonso litentha mulu okwanira muyeso wa ma milioni anayi pa mphindi kupereka kutentha ndi kuwala komwe nkofunika kwambiri kuti ife tikhale ndi moyo, momwemonso mtima wathu umagunda kwa 2.5 biliyoni nthawi yonse ya moyo wathu popanda kupumula. Nkotani kuti munthu – yemwe ali opindula kwambiri muzonse izi kukana choonadi ichi chomwe chili chomufikitsa ku chisomo chakuthekera kwa Namalenga.
2. Kulandira Mosiyana Ndi Choonacho.
Kwa iwo omwe aumilira kukana umboni uwu. mkwiyo wa Mulungu uzavumbulutsidwa pa iwo, Mulungu anapereka umboni okwanira – kudzera mwa munthu mwini – komanso kudzera ku chilengedwe chonse. Pamene Mzimu Woyera akuti, “Palibenso” Ndiye kuti palibenso mpata wina operekedwa kachikena. Koma kwa omwe avomeredza za umboni wa Mulungu ali a paderadera – ngakhale kuti iwo sanamve kale za Uthenga Wabwino – Ngati aika mtima pa Yemwe analenga zinthu zonse ndi kumufuna Iye ndi mtima oona, Mulungu azatsegula kwa iwo njira ya chipulumutso.
3. Chikondi Chopatsidwa Chosoweka Kusamalitsa.
Maumboni osawerengeka akhala akusimikidzira kudzera mu chirengedwe chonse kuvumbulutsa za kufunisitsa kwa Mulungu kugwira ntchito yowombola anthu onse, kwa onse tinalandira kale chikondi ichi, malawi otentha a dzuwa ndi dontho la mvura silinganyamulitse kanthu kotsamwitsa mumoyo wathu – mu zonse izi – timaimabe mu mphamvu Yake yosaneneka ndi chikondi chopatsidwa chosowekera kusamalitsa. Zikachitika izi, miyoyo yotizungulira – nayonso – izatha kumudzindikira Mulungu kudzera mu umboni odabwitsa onga uwu. Kuima modzichepetsa pansi pa ulemerero wa Mulungu omwe zolengedwa zonse zimalengedza, tiyeni tiyende mu moyo okondwera mwa chisomo chonse chonga ichi.
Novembala 30, 2025 Utumiki wa Tsiku la Ambuye
Chivumbulutso cha Mulungu Choonekera mwa Zinthu Zolengedwa
Aroma 1:20
Abusa Sung-Hyun Kim



